1. Ndinati mumtima mwanga, Tiyetu, ndikuyese ndi cimwemwe; tapenya tsono zabwino; ndipo taona, icinso ndi cabe.
2. Ndinati, Kuseka ndi misala; ndi cimwemwe kodi cicita ciani?
3. Ndinafuna mumtima mwanga kusangalatsa thupi langa ndi vinyo, mtima wanga ulikunditsogolera mwanzeru, ndi kugwira utsiru, kuti ndizindikire cabwinoco ca ana a anthu nciani cimene azicicita pansi pa thambo masiku onse a moyo wao.
4. Ndinadzipangira zazikuru; ndinadzimangira nyumba; ndi kunka mipesa;