9. Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.
10. Citsulo cikakhala cosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pocenjeza.
11. Njoka ikaluma isanalodzedwe, watsenga saona mphotho.
12. Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga cisomo; koma milomo ya citsiru idzacimeza.
13. Ciyambi ca mau a m'kamwa mwace ndi utsiru; ndipo cimariziro ca m'kamwa mwace ndi misala yoipa,