Mlaliki 10:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.

10. Citsulo cikakhala cosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pocenjeza.

11. Njoka ikaluma isanalodzedwe, watsenga saona mphotho.

12. Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga cisomo; koma milomo ya citsiru idzacimeza.

13. Ciyambi ca mau a m'kamwa mwace ndi utsiru; ndipo cimariziro ca m'kamwa mwace ndi misala yoipa,

Mlaliki 10