Mlaliki 10:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ngati mkuru akukwiyira, usasiye malo ako; cifukwa cifatso cipembedza utacimwa kwambiri.

5. Pali coipa ndaciona pansi pano, ngati kulakwa koyambira ndi mkuru;

6. utsiru ukhazikika pamwamba penipeni, ndipo olemera angokhala mwamanyazi.

7. Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, ndi mafumu, alikuyenda pansi ngati akapolo.

8. Wokumba mbuna adzagwamo; ndipo woboola mpanda njoka idzamluma.

9. Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.

Mlaliki 10