3. Inde, poyendanso citsiru panjira, nzeru yace imthera ndipo angoti kwa onse kuti, Ndine citsiru.
4. Ngati mkuru akukwiyira, usasiye malo ako; cifukwa cifatso cipembedza utacimwa kwambiri.
5. Pali coipa ndaciona pansi pano, ngati kulakwa koyambira ndi mkuru;
6. utsiru ukhazikika pamwamba penipeni, ndipo olemera angokhala mwamanyazi.