4. Mbadwo wina opita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse,
5. inde dzuwa lituruka, nililowa, nilifulumira komwe linaturukako.
6. Kulowa kumwela ndi kuzungulira: kumpoto zungulire zungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ace.
7. Mitsinje yonse ithira m'nyanja, koma nyanja yosadzala; komwe imukira mitsinjeyo, komweko ibweranso.