Miyambi 8:13-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.

15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.

16. Mwa ine akalonga ayang'anira,Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,

17. Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.

18. Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.

19. Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka;Phindu langa liposa siliva wosankhika.

20. Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,

21. Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.

22. Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.

23. Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.

Miyambi 8