Miyambi 8:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti nzeru iposa ngale,Ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo,

12. Ine Nzeru ndikhala m'kucenjera, ngati m'nyumba yanga;Ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

13. Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

14. Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.

15. Mwa ine mafumu alamulira;Akazembe naweruza molungama.

Miyambi 8