Miyambi 7:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Watenga thumba la ndalama m'dzanja lace,Tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21. Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace,Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22. Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa;Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

23. Mpaka mubvi ukapyoza mphafa yace;Amtsata monga mbalame yotamangira msampha;Osadziwa kuti adzaononga moyo wace.

24. Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,Labadirani mau a m'kamwa mwanga.

25. Mtima wako usapatukire ku njira ya mkaziyo,Usasocere m'mayendedwe ace.

26. Pakuti amagwetsa ambiri, atawalasa;Ndipo ophedwa ndi iye acurukadi.

27. Nyumba yace ndiyo njira ya kumanda,Yotsikira ku zipinda za imfa.

Miyambi 7