Miyambi 7:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Tiye tikondwere ndi cikondano mpaka mamawa;Tidzisangalatse ndi ciyanjano.

19. Pakuti mwamuna kulibe kwathu,Wapita ulendo wa kutari;

20. Watenga thumba la ndalama m'dzanja lace,Tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21. Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace,Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22. Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa;Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

23. Mpaka mubvi ukapyoza mphafa yace;Amtsata monga mbalame yotamangira msampha;Osadziwa kuti adzaononga moyo wace.

Miyambi 7