5. Dzipulumutse wekha ngati mphoyo ku dzanja la msaki,Ndi mbalame ku dzanja la msodzi.
6. Pita kunyerere, wolesi iwe,Penya njira zao nucenjere;
7. Ziribe mfumu,Ngakhale kapitao, ngakhale mkuru;
8. Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe;Nizituta dzinthu zao m'masika.
9. Udzagona mpaka liti, wolesi iwe?Udzauka ku tulo tako liti?
10. Tulo ta pang'ono, kuodzera pang'ono,Kungomanga manja pang'ono, ndi kugona;
11. Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.