Miyambi 31:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mtima wa mwamuna wace umkhulupirira,Sadzasowa phindu.

12. Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa,Masiku onse a moyo wace.

13. Afuna ubweya ndi thonje,Nacita mofunitsa ndi manja ace.

14. Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.

15. Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.

16. Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.

Miyambi 31