Miyambi 29:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Yemwe alera kapolo wace mwa ufulu kuyambira ubwana wace,Pambuyo pace adzadziyesa mwana wobala.

22. Mwamuna wamkwiyo aputa makangano;Waukali acuruka zolakwa.

23. Kudzikuza kwa munthu kudzamcepetsa;Koma wokhala ndi mtima wodzicepetsa adzalemekezedwa.

24. Woyenda ndi mbala ada moyo wace wace;Amva kulumbira, koma osaulula kanthu.

25. Kuopa anthu kuchera msampha;Koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka,

26. Ambiri afunafuna ciyanjano ca mkuru;Koma ciweruzo ca munthu cicokera kwa Yehova.

27. Munthu woipa anyansa olungama;Ndipo woongoka m'njira anyansa wocimwa.

Miyambi 29