Miyambi 28:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Wosoceretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa,Adzagwa mwini m'dzenje lace;Koma angwiro adzalandira colowa cabwino.

11. Wolemera adziyesa wanzeru;Koma wosauka wozindikira aululitsa zace.

12. Posekera olungama pali ulemerero wambiri;Koma pouka oipa anthu amabisala.

13. Wobisa macimo ace sadzaona mwai;Koma wakuwabvomereza, nawasiya adzacitidwa cifundo.

14. Wodala munthu wakuopakosalekeza;Koma woumitsa mtima wace adzagwa m'zoipa.

Miyambi 28