Miyambi 27:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Wofuna kumletsayo afuna kuletsa mphepo;Dzanja lace lamanja lingogwira mafuta.

17. Citsulo cinola citsulo;Comweco munthu anola nkhope ya mnzace.

18. Wosunga mkuyu adzadya zipatso zace;Wosamalira ambuyace adzalemekezedwa.

19. Monga m'madzi nkhope zionana,Momwemo mitima ya anthu idziwana.

20. Kunsi kwa manda ndi kucionongeko sikukhuta;Ngakhale maso a munthu sakhutai.

21. Siliva asungunuka m'mbiya,Ndi golidi m'ng'anjo,Motero comwe munthu acitama adziwika naco.

22. Ungakhaleukonolacitsirum'mtondo ndi munsi, pamodzi ndi mphale,Koma utsiru wace sudzamcoka.

23. Udziwitsitse zoweta zako ziri bwanji,Samalira magulu ako;

Miyambi 27