11. Mwananga, khala wanzeru, nukondweretse mtima wanga;Kuti ndimuyankhe yemwe anditonza.
12. Wocenjera aona zoipa, nabisala;Koma acibwana angopitirira, nalipitsidwa.
13. Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi waciwerewere cikole umgwire mwini.
14. Yemwe adalitsa mnzace ndi mau akuru pouka mamawa,Anthu adzaciyesa cimeneco temberero.