Miyambi 27:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usanyadire zamawa,Popeza sudziwa tsiku lina lidzabala ciani?

2. Wina akutame, si m'kamwamwako ai;Mlendo, si milomo ya iwe wekha.

3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.

4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?

5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.

6. Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika;Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.

Miyambi 27