13. Wolesi ati, Mkango uli panjira,Wobangulawo uli m'makwalala.
14. Monga citseko cikankhikira pa zitsulo za pamphuthu,Momwemo wolesi agubuduka pakama pace.
15. Wolesi alonga dzanja lace m'mbale;Kumtopetsa kulibweza kukamwa kwace.
16. Wolesi adziyesa wanzeruKoposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.