Miyambi 25:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa,Momwemo mau abwino akucokera ku dziko lakutari.

26. Monga kasupe wopondedwa, ndi citsime cobvonongeka,Momwemo wolungama ngati akonjera woipa.

27. Kudya uci wambiri sikuli kwabwino;Comweco kufunafuna ulemu wako wako sikuli ulemu.

28. Wosalamulira mtima waceAkunga mudzi wopasuka wopanda linga,

Miyambi 25