Miyambi 25:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Monga wobvula maraya tsiku lamphepo,Ngakhale kuthira vinyo wosasa m'soda,Momwemo woyimbira nyimbo munthu wacisoni.

21. Mdani wako akamva njala umdyetse,Akamva ludzu ummwetse madzi,

22. Pakuti udzaunjika makala amoto pamtu pace;Ndipo Yehova adzakupatsa mphotho,

23. Mphepo ya kumpoto ifikitsa mvula;Comweco lilime losinjirira likwiyitsa nkhope.

24. Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunikaKuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

25. Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa,Momwemo mau abwino akucokera ku dziko lakutari.

Miyambi 25