Miyambi 22:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

11. Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.

12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.

14. M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.

15. Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.

16. Wotsendereza waumphawi kuti acurukitse cuma cace,Ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.

17. Chera makutu ako, numvere mau a anzeru,Nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

18. Pakuti mauwo akondweretsa ngati uwasunga m'kati mwako,Ngati akhazikika pamodzi pa milomo yako.

19. Ndakudziwitsa amenewo lero, ngakhale iwedi,Kuti ukhulupirire Yehova.

20. Kodi sindinakulembera zoposa Za uphungu ndi nzeru;

21. Kuti ukadziwitse ntheradi yace ya mau oona,Nukabwere ndi mau oona kwa iwo amene anakutumiza?

22. Usalande za waumphawi cifukwa ali waumphawi,Ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.

23. Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao;Omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.

24. Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga;Ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;

Miyambi 22