Miyambi 22:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Wolemera alamulira osauka;Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8. Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

Miyambi 22