22. Usalande za waumphawi cifukwa ali waumphawi,Ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.
23. Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao;Omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.
24. Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga;Ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;
25. Kuti ungaphunzire mayendedwe ace,Ndi kutengera moyo wako msampha,
26. Usakhale wodulirana mpherere,Ngakhale kumperekera cikole ca ngongole zace.