9. Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,Ndayera opanda cimo?
10. Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.
11. Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.
12. Khutu lakumva, ndi diso lopenya,Yehova anapanga onse awiriwo.
13. Usakonde tulo ungasauke;Phenyula maso, udzakhuta zakudya.
14. Wogula ati, Cacabe cimeneco.Koma atacoka adzitama.