Miyambi 20:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu;Koma zitsiru zonse zimangokangana,

4. Wolesi salima cifukwa ca cisanu;Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

5. Uphungu wa m'mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya;Koma munthu wozindikira adzatungapo,

6. Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace;Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.

8. Mfumu yokhala pa mpando waweruziraIpitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

Miyambi 20