Miyambi 20:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Vinyo acita ciphwete, cakumwa caukali cisokosa;Wosocera nazo alibe nzeru.

2. Kuopsya kwa mfumu ndiko kubangula kwa mkango;Womputa acimwira moyo wace wace.

3. Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu;Koma zitsiru zonse zimangokangana,

4. Wolesi salima cifukwa ca cisanu;Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

Miyambi 20