Miyambi 2:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Kukupulumutsa ku njira yoipa,Kwa anthu onena zokhota;

13. Akusiya mayendedwe olungama,Akayende m'njira za mdima;

14. Omwe asangalala pocita zoipa,Nakondwera ndi zokhota zoipa;

15. Amene apotoza njira zao,Nakhotetsa mayendedwe ao;

16. Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere,Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

17. Wosiya bwenzi la ubwana wace,Naiwala cipangano ca Mulungu wace;

18. Nyumba yace itsikira kuimfa,Ndi mayendedwe ace kwa akufa;

19. Onse akunka kwa iye sabweranso,Safika ku njira za moyo;

Miyambi 2