6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.
7. Abale onse a wosauka amuda;Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye?Awatsata ndi mau, koma kuli zi.
8. Wolandira nzeru akonda moyo wace;Wosunga luntha adzapeza zabwino.
9. Mboni yonama sidzapulumuka cilango;Wolankhula mabodza adzaonongeka.
10. Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?
11. Kulingalira kwa munthu kucedwetsa mkwiyo;Ulemerero wace uli wakuti akhululukire colakwa.
12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.