4. Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.
5. Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,Ngakhale kucitira cetera wolungama.
6. Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.
7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.
8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.