Miyambi 18:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.

13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.

14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16. Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.

17. Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama;Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.

18. Ula uletsa makangano,Nulekanitsa amphamvu.

19. Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

Miyambi 18