Miyambi 16:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Zonse Yehova anazipangaziri ndi zifukwa zao;Ngakhale amphulupulu kuti aone tsiku loipa,

5. Yense wonyada mtima anyansa Yehova;Zoonadi sadzapulumuka cilango.

6. Mphulupulu iomboledwa ndi cifundo ndi ntheradi;Apatuka pa zoipa poopa Yehova.

7. Njira za munthu zikakonda Yehova,Ayanjanitsana naye ngakhale adani ace.

8. Zapang'ono, pokhala cilungamo,Ziposa phindu lalikuru lopanda ciweruzo.

Miyambi 16