Miyambi 16:25-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka,Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

26. Wanchito adzigwirira yekha nchito;Pakuti m'kamwa mwace mumfulumiza.

27. Munthu wopanda pace akonzeratu zoipa;Ndipo m'milomo mwace muli moto wopsereza.

28. Munthu wokhota amautsa makani;Kazitape afetsa ubwenzi.

29. Munthu waciwawa akopa mnzace,Namuyendetsa m'njira yosakhala bwino.

30. Wotsinzina ndiye aganizira zakhota;Wosunama afikitsa zoipa.

31. Imvi ndiyo korona wa ulemu,Idzapezedwa m'njira ya cilungamo.

32. Wosakwiya msanga aposa wamphamvu;Wolamulira mtima wace naposa wolanda mudzi.

33. Maere aponyedwa pamfunga;Koma ndiye Yehova alongosola zonse.

Miyambi 16