20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.
21. Wanzeru mtima adzachedwa wocenjera;Ndipo kukoma kwa milomo kuyenjezera kuphunzira.
22. Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wace;Koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.
23. Mtima wa wanzeru ucenjeza m'kamwa mwace,Nuphunzitsanso milomo yace.