15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.
16. Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golidi,Kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?
17. Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.
18. Kunyada kutsogolera kuonongekaMtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.
19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.
20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.