8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.
9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.
10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.
11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?