Miyambi 15:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.

10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.

11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

Miyambi 15