Miyambi 15:22-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.

23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?

24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.

25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,

26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.

29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.

Miyambi 15