22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,
26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.
27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.
28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.
29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.