Miyambi 15:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.

21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.

Miyambi 15