12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.
13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.
14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.
18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.
19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.