Miyambi 14:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Popanda zoweta modyera muti see;Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.

5. Mboni yokhulupirika sidzanama;Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

6. Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.

7. Pita pamaso pa munthu wopusa,Sudzazindikira milomo yakudziwa.

8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

Miyambi 14