Miyambi 14:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

20. Waumphawi adedwa ndi anzace omwe;Koma akukonda wolemera acuruka.

Miyambi 14