12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.
13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.
14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.
15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.
16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.
17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.
18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.
19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.