Miyambi 14:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

Miyambi 14