9. Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.
10. Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.
11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.
12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.