Miyambi 12:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

18. Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19. Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20. Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa;Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21. Palibe bvuto lidzagwera wolungama;Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

22. Milomo yonama inyansa Yehova;Koma ocita ntheradi amsekeretsa.

23. Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24. Dzanja la akhama lidzalamulira;Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,

Miyambi 12