1. Wokonda mwambo akonda kudziwa;Koma wakuda cidzudzulo apulukira.
2. Yehova akomera mtima munthu wabwino;Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,
3. Munthu sadzakhazikika ndi udio,Muzu wa olungama sudzasunthidwa.
4. Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.
5. Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.