22. Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.
23. Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.
24. Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.
25. Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.
26. Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.
27. Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.