Miyambi 11:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Wopeputsa mnzace asowa nzeru;Koma wozindikira amatonthola.

13. Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;Koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14. Popanda upo wanzeru anthu amagwa;Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.

15. Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo;Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.

Miyambi 11