Miyambi 11:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Muyeso wonyenga unyansa Yehova;Koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2. Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;Koma nzeru iri ndi odzicepetsa,

3. Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;Koma kukhota kwa aciwembu kudzawaononga.

4. Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo;Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

5. Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.

6. Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7. Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka;Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.

8. Wolungama apulumuka kubvuto;Woipa nalowa m'malo mwace.

Miyambi 11