Miyambi 1:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27. Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28. Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;

Miyambi 1