Mateyu 3:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo masiku aja anadza Yohane Mbatizi, nalalikira m'cipululu ca Yudeya,

2. nanena, Tembenukani mitima; cifukwa Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

3. Pakuti uyu ndiye ananenayo Yesaya mneneri, kuti,Mau a wopfuula m'cipululu,Konzani khwalala la Ambuye,Lungamitsani njira zace.

4. Ndipo Yohane yekhayo anali naco cobvala cace ca ubweya wangamila, ndi lamba lacikopa m'cuuno mwace; ndi cakudya cace cinali dzombe ndi uci wa kuthengo.

5. Pamenepo panamturukira iye ku Yerusalemu, ndi Yudeya lonse, ndi dziko lonse loyandikana ndi Yordano;

6. nabatizidwa ndi iye mu mtsinjewo wa Yordano, alikuulula macimo ao.

Mateyu 3