58. yemweyo anapita kwa Pilato, napempha mtembo wa Yesu. Pomwepo Pilato analamula kuti uperekedwe.
59. Ndipo Yosefe anatenga mtembo, naukulunga m'nsaru yabafuta yoyeretsa,
60. 14 nauika m'manda ace atsopano, osemedwa m'mwala, nakunkhunizira mwala waukuru pakhomo pa manda, nacokapo,
61. Ndipo Mariya wa Magadala anali pamenepo, ndi Mariya winayo, anakhala pansi popenyana ndi mandawoo
62. Ndipo m'mawa mwace, ndilo dzuwa lotsatana ndi tsiku lokonzera, ansembe akuru ndi Afarisi anasonkhanira kwa Pilato,
63. nanena, Mfumu, takumbukira ife kuti wonyenga uja anati, pamene anali ndi moyo, 15 Ndidzaukapofikamasikuatatu.
64. Cifukwa cace mulamule kuti asindikize pamandapo, kufikira tsiku lacitatulo, kuti kapena ophunzira ace angadze, nadzamuba Iye, nadzanena kwa anthu, kuti Iye anauka kwa akufa: ndipo cinyengo comariza cidzaposa coyambaco.
65. Pilato anati kwa iwo, Tengani alonda; mukani, kasungeni monga mudziwa.
66. Ndipo iwo anamuka, nasunga manda, 16 nasindikizapo cizindikiro pamwalapo, iwo pamodzi ndi alondawo.