34. anamwetsa Iye vinyo wosanganiza ndi ndulu; ndipo Iye, m'mene analawa, sanafuna kumwa.
35. Ndipo pamene anampacika Iye, anagawana zobvala zace ndi kulota maere:
36. nakhala iwo pansi, namdikira kumeneko.
37. Ndipo anaika pamwamba pamutu pace liwongo lace lolembedwa: UYU NDI YESU MFUMU YA AYUDA.
38. Pamenepo anapacika pamodzi ndi Iyeacifwamba awiri, mmodzi ku dzanja lamanja, ndi wina kulamanzere.
39. Ndipo anthu akupitirirapo 1 anamcitira mwano Iye ndi kupukusa mitu yao,
40. nati, Nanga 2 Iwe, wopasula Kacisi, ndi kummanganso masiku atatu, tadzipulumutsa wekha; 3 ngati uli Mwana wa Mulungu, tatsika pamtandapo.
41. Comweconso ansembe akuru, pamodzi ndi alembi ndi akuru anamcitira cipongwe, nati,
42. Anapulumutsa ena, sangathe kudzipulumutsa yekha. Ndiye Mfumu ya Ayuda; atsike tsopano pamtandapo, ndipo tidzamkhulupirira Iye.